1
Lk. 17:19
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
Kenaka Yesu adauza munthuyo kuti, “Nyamuka, pita. Chikhulupiriro chako chakuchiritsa.”
Параўнаць
Даследуйце Lk. 17:19
2
Lk. 17:4
Akakuchimwira kasanunkaŵiri pa tsiku, nabwera kasanunkaŵiri kudzanena kuti, ‘Pepani,’ umkhululukire ndithu.”
Даследуйце Lk. 17:4
3
Lk. 17:15-16
Tsono mmodzi mwa iwo, ataona kuti wachira, adabwerera nayamba kuyamika Mulungu mokweza mau. Adagwada nkuŵerama kwambiri pamaso pa Yesu, namthokoza. Koma munthuyo anali Msamariya.
Даследуйце Lk. 17:15-16
4
Lk. 17:3
Chenjerani tsono! “Mbale wako akachimwa, umdzudzule. Akatembenuka mtima, umkhululukire.
Даследуйце Lk. 17:3
5
Lk. 17:17
Apo Yesu adati, “Kodi achira aja si khumi? Nanga asanu ndi anai ena aja ali kuti?
Даследуйце Lk. 17:17
6
Lk. 17:6
Koma Ambuye adati, “Mukadakhala ndi chikhulupiriro ngakhale chochepa kwambiri ngati kambeu ka mpiru, bwenzi mutauza mkuyu uwu kuti, ‘Zuka, kadzibzale m'nyanja,’ ndipo ukadakumverani ndithu.”
Даследуйце Lk. 17:6
7
Lk. 17:33
Aliyense woyesa kudzisungira moyo wake, adzautaya, koma woutaya adzausunga.
Даследуйце Lk. 17:33
8
Lk. 17:1-2
Yesu adauza ophunzira ake kuti, “Zochimwitsa anthu sizingalephere kuwoneka, koma tsoka kwa munthu wobwera nazoyo. Kukadakhala kwabwino kuti ammangirire chimwala cha mphero m'khosi ndi kukamponya m'nyanja, kupambana kuti achimwitse mmodzi mwa ana ang'onoang'onoŵa.
Даследуйце Lk. 17:1-2
9
Lk. 17:26-27
“Monga momwe zidaachitikira pa nthaŵi ya Nowa, zidzateronso pa nthaŵi ya Mwana wa Munthu. Masiku amenewo anthu ankangodya ndi kumwa, ankakwatira ndi kumakwatiwa, mpaka tsiku limene Nowa adaloŵa m'chombo. Pamenepo chigumula chidafika nkuŵaononga onse.
Даследуйце Lk. 17:26-27
Стужка
Біблія
Пляны чытаньня
Відэа