1
Lk. 19:10
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
Pajatu Mwana wa Munthu adabwera kudzafunafuna ndi kudzapulumutsa amene adatayika.”
Параўнаць
Даследуйце Lk. 19:10
2
Lk. 19:38
Adati, “Ndi yodala Mfumu imene ilikudza m'dzina la Ambuye. Mtendere Kumwamba, ulemu kwa Mulungu kumwambamwamba.”
Даследуйце Lk. 19:38
3
Lk. 19:9
Apo Yesu adamuuza kuti, “Chipulumutso chafika m'banja lino lero, popeza kuti ameneyunso ndi mwana wa Abrahamu.
Даследуйце Lk. 19:9
4
Lk. 19:5-6
Ndiye pamene Yesu adafika pamalopo, adayang'ana m'mwamba, namuuza kuti, “Zakeyo, fulumira, tsika, chifukwa lero ndikuyenera kukakhala nao kunyumba kwako.” Pompo Zakeyo adafulumira, natsika, kenaka nkukamlandiradi Yesu mokondwa kwambiri.
Даследуйце Lk. 19:5-6
5
Lk. 19:8
Koma Zakeyo adaimirira nauza Ambuye kuti, “Ambuye, ndithudi ndidzapereka hafu la chuma changa kwa amphaŵi. Ndipo ngati ndidalandira kanthu kwa munthu aliyense monyenga, ndidzamubwezera kanai.”
Даследуйце Lk. 19:8
6
Lk. 19:39-40
Apo Afarisi ena amene adaali m'khamumo adauza Yesu kuti, “Aphunzitsi, auzeni ophunzira anuŵa aleke zimenezi.” Iye adati, “Ndikutitu iwoŵa akangokhala chete, ifuula ndi miyalayi.”
Даследуйце Lk. 19:39-40
Стужка
Біблія
Пляны чытаньня
Відэа