1
GENESIS 9:12-13
Buku Lopatulika
Ndipo anati Mulungu, Ichi ndi chizindikiro cha pangano limene ndipangana ndi Ine ndi inu, ndi zamoyo zonse zili pamodzi ndi inu, ku mibadwomibadwo; ndiika utawaleza wanga m'mtambomo, ndipo udzakhala chizindikiro cha pangano lopangana ndi Ine ndi dziko lapansi.
השווה
חקרו GENESIS 9:12-13
2
GENESIS 9:16
Ndipo utawo udzakhala m'mtambo; ndipo ndidzauyang'anira kuti ndikumbukire pangano lachikhalire lili ndi Mulungu ndi zamoyo zonse zokhala ndi moyo padziko lapansi.
חקרו GENESIS 9:16
3
GENESIS 9:6
Amene akhetsa mwazi wa munthu, ndi munthunso mwazi wake udzakhetsedwa: chifukwa m'chifanizo cha Mulungu Iye anampanga munthu.
חקרו GENESIS 9:6
4
GENESIS 9:1
Ndipo Mulungu anadalitsa Nowa ndi ana ake, nati kwa iwo, Mubalane, muchuluke, mudzaze dziko lapansi.
חקרו GENESIS 9:1
5
GENESIS 9:3
Zoyenda zonse zamoyo zidzakhala zakudya zanu; monga therere laliwisi ndakupatsani inu zonsezo.
חקרו GENESIS 9:3
6
GENESIS 9:2
Kuopsa kwanu, ndi kuchititsa mantha kwanu kudzakhala pa zinyama zonse za dziko lapansi, ndi pa zouluka zonse za m'mlengalenga, ndi pa zonse zokwawa pansi, ndi pansomba zonse za m'nyanja, zapatsidwa m'dzanja lanu.
חקרו GENESIS 9:2
7
GENESIS 9:7
Ndi inu, mubalane, muchuluke; muswane padziko lapansi, nimuchuluke m'menemo.
חקרו GENESIS 9:7
בית
כתבי הקודש
תכניות
קטעי וידאו