1
GENESIS 15:6
Buku Lopatulika
Ndipo anakhulupirira Yehova, ndipo kunayesedwa kwa iye chilungamo.
比較
GENESIS 15:6で検索
2
GENESIS 15:1
Zitapita izo, mau a Yehova anadza kwa Abramu m'masomphenya, kuti, Usaope, Abramu, Ine ndine chikopa chako ndi mphotho yako yaikulukulu.
GENESIS 15:1で検索
3
GENESIS 15:5
Ndipo anamtulutsa iye kunja, nati, Tayang'anatu kumwamba, uwerenge nyenyezi, ngati ukhoza kuziwerenga zimenezo: ndipo anati kwa iye, Zoterezo zidzakhala mbeu zako.
GENESIS 15:5で検索
4
GENESIS 15:4
Ndipo, taonani, mau a Yehova anadza kwa iye kuti, Uyu sadzakhala wakulowa m'malo mwako; koma iye amene adzatuluka m'chuuno mwako, ndiye adzakhala wakulowa m'malo mwako.
GENESIS 15:4で検索
5
GENESIS 15:13
Ndipo anati kwa Abramu, Dziwitsa ndithu kuti mbeu zako zidzakhala alendo m'dziko la eni, ndipo zidzatumikira iwo, ndipo iwo adzasautsa izo zaka mazana anai
GENESIS 15:13で検索
6
GENESIS 15:2
Ndipo Abramu anati, Ambuye Mulungu, mudzandipatsa ine chiyani popeza ndine wopanda mwana, ndi amene adzakhala mwini nyumba yanga ndiye Eliyezere wa ku Damasiko?
GENESIS 15:2で検索
7
GENESIS 15:18
Tsiku lomwelo Yehova anapangana chipangano ndi Abramu, nati, Ndidzapatsa mbeu zako dziko ili, kuyambira pamtsinje wa ku Ejipito kufikira pamtsinje waukulu, mtsinje wa Yufurate
GENESIS 15:18で検索
8
GENESIS 15:16
Koma iwo adzabweranso kuno mbadwo wachinai: pakuti mphulupulu za Aamori sizinakwaniridwe.
GENESIS 15:16で検索
ホーム
聖書
読書プラン
ビデオ