Erika, USA

Erika, USA

Ndinali wolowedwa ndi mankhwala odetsa kwa zaka zoposa 10, ndipo ndinataya chilichonse. Ndinalinso kuyesa kudya mankhwala ochuluka mwadala, chifukwa ndinamva kuti sindinali ndi chilichonse chosalira moyo. Sindinafune kumva chilichonse chokhudza Mulungu, chifukwa ndinali ndi mkwiyo ndi chidani. Ndinali wotayika ndipo ndinali ndekha ndipo sindinadziwe momwe angakonzedwe moyo wanga. Chimene sindinadziwe pa nthawi imeneyo chinali chakuti sikunali momwe angakonzedwe moyo wanga--chinali Ndani amene angathe kuukonza.

Kwa pafupifupi zaka ziwiri tsopano, ndaona kusintha mwa ine komwe ndingapereke ulemu wake kwa Yesu basi. Kudzera mu Vesi la Tsiku, Malemba Oongozedwa, ndi Mapulogalamu, nasangalala kukula pafupi ndi Mulungu ndi kulimbitsa maziko anga mwa Iye. Ndimapeza chodziwitsa cha Vesi la Tsiku, ndipo chimandikumbutsa kuwerenga Baibulo langa mmawa uliwonse. Tsopano, ndikuyang'ana m'mbuyo ndikuona kuti Iye anali nane nthawi yonse, akungodikira kuti ndimulole kulowa.