1
GENESIS 9:12-13
Buku Lopatulika
Ndipo anati Mulungu, Ichi ndi chizindikiro cha pangano limene ndipangana ndi Ine ndi inu, ndi zamoyo zonse zili pamodzi ndi inu, ku mibadwomibadwo; ndiika utawaleza wanga m'mtambomo, ndipo udzakhala chizindikiro cha pangano lopangana ndi Ine ndi dziko lapansi.
Karşılaştır
GENESIS 9:12-13 keşfedin
2
GENESIS 9:16
Ndipo utawo udzakhala m'mtambo; ndipo ndidzauyang'anira kuti ndikumbukire pangano lachikhalire lili ndi Mulungu ndi zamoyo zonse zokhala ndi moyo padziko lapansi.
GENESIS 9:16 keşfedin
3
GENESIS 9:6
Amene akhetsa mwazi wa munthu, ndi munthunso mwazi wake udzakhetsedwa: chifukwa m'chifanizo cha Mulungu Iye anampanga munthu.
GENESIS 9:6 keşfedin
4
GENESIS 9:1
Ndipo Mulungu anadalitsa Nowa ndi ana ake, nati kwa iwo, Mubalane, muchuluke, mudzaze dziko lapansi.
GENESIS 9:1 keşfedin
5
GENESIS 9:3
Zoyenda zonse zamoyo zidzakhala zakudya zanu; monga therere laliwisi ndakupatsani inu zonsezo.
GENESIS 9:3 keşfedin
6
GENESIS 9:2
Kuopsa kwanu, ndi kuchititsa mantha kwanu kudzakhala pa zinyama zonse za dziko lapansi, ndi pa zouluka zonse za m'mlengalenga, ndi pa zonse zokwawa pansi, ndi pansomba zonse za m'nyanja, zapatsidwa m'dzanja lanu.
GENESIS 9:2 keşfedin
7
GENESIS 9:7
Ndi inu, mubalane, muchuluke; muswane padziko lapansi, nimuchuluke m'menemo.
GENESIS 9:7 keşfedin
Ana Sayfa
Kutsal Kitap
Okuma Planları
Videolar