1
GENESIS 25:23
Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014
BLPB2014
Yehova ndipo anati kwa iye, Mitundu iwiri ili m'mimba mwako, magulu awiri a anthu adzatuluka m'mimba mwako; gulu lina lidzapambana mphamvu ndi linzake; wamkulu adzakhala kapolo wa wamng'ono.
مقایسه
GENESIS 25:23 را جستجو کنید
2
GENESIS 25:30
ndipo Esau anati kwa Yakobo, Undipatse ndidye chofiiracho; chifukwa ndalefuka: chifukwa chake anamutcha dzina lake Edomu.
GENESIS 25:30 را جستجو کنید
3
GENESIS 25:21
Ndipo Isaki anampembedzera mkazi wake kwa Yehova popeza anali wouma: ndipo Yehova analola kupembedza kwake, ndipo Rebeka mkazi wake anatenga pakati.
GENESIS 25:21 را جستجو کنید
4
GENESIS 25:32-33
Ndipo Esau anati, Taona, ine ndifuna kufa: ukuluwo ndidzapindulanji nao? Ndipo anati Yakobo, Undilumbirire ine lero lomwe, ndipo analumbirira iye; nagulana ndi Yakobo ukulu wake.
GENESIS 25:32-33 را جستجو کنید
5
GENESIS 25:26
Pambuyo pake ndipo anabadwa mphwake ndipo dzanja lake linagwira chitende cha Esau, ndi dzina lake linatchedwa Yakobo: ndipo Isaki anali wa zaka makumi asanu ndi limodzi pamene mkazi wake anabala iwo.
GENESIS 25:26 را جستجو کنید
6
GENESIS 25:28
Ndipo Isaki anakonda Esau, chifukwa anadya nyama yake ya m'thengo; koma Rebeka anakonda Yakobo.
GENESIS 25:28 را جستجو کنید