1
Lk. 13:24
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
“Yesetsani kuloŵera pa khomo lophaphatiza, pakuti kunena zoona anthu ambiri adzafuna kuloŵa, koma adzalephera.
Сравни
Разгледайте Lk. 13:24
2
Lk. 13:11-12
M'menemo munali mai wina amene anali ndi mzimu woipa umene udamudwalitsa zaka 18. Anali ndi msana wokhota, mwakuti sankatha konse kuŵeramuka. Pamene Yesu adamuwona, adamuitana namuuza kuti, “Mai inu, mwamasuka ku matenda anu.”
Разгледайте Lk. 13:11-12
3
Lk. 13:13
Adamsanjika manja, ndipo pompo maiyo adaongoka, nayamba kutamanda Mulungu.
Разгледайте Lk. 13:13
4
Lk. 13:30
Pamenepo amene ali otsirizira adzakhala oyambirira, ndipo amene ali oyambirira adzakhala otsirizira.”
Разгледайте Lk. 13:30
5
Lk. 13:25
“Mwini nyumba adzanyamuka nkutseka pa khomo. Pamenepo, okhala panjanu mudzayamba kugogoda nkumanena kuti, ‘Ambuye, titsekulireni.’ Koma Iye adzakuyankhani kuti, ‘Sindikudziŵa kumene mukuchokera.’
Разгледайте Lk. 13:25
6
Lk. 13:5
Iyai, koma mukapanda kutembenuka mtima, inunso mudzaonongedwa ngati iwo aja.”
Разгледайте Lk. 13:5
7
Lk. 13:27
Koma Iye adzakuuzani kuti, ‘Pepani, sindikudziŵa kumene mukuchokera. Chokani apa nonsenu, anthu ochita zoipa.’
Разгледайте Lk. 13:27
8
Lk. 13:18-19
Yesu adati, “Kodi Ufumu wa Mulungu uli ngati chiyani, ndipo ndingauyerekeze ndi chiyani? Uli ngati njere ya mbeu ya mpiru imene munthu adakaifesa m'munda mwake. Idamera nisanduka mtengo, mbalame zamumlengalenga nkumabwera kudzamanga zisa pa nthambi zake.”
Разгледайте Lk. 13:18-19
Начало
Библия
Планове
Видеа