Koma ngati nthambi zina zinathyoledwa, ndipo iwe, ndiwe mtengo wa azitona wa kuthengo, unalumikizidwa mwa izo, nugawana nazo za muzu za mafuta ake a mtengowo, usadzitama iwe wekha pa nthambizo: koma ngati udzitama wekha, suli iwe amene unyamula muzu, ai, koma muzu ukunyamula iwetu.